Home » Lyrics » Bertha Nkhoma – Chipambano Lyrics

Bertha Nkhoma – Chipambano Lyrics

by Malawi Gospel Music
714 views

Chorus

Pamene mukapanga za ine
Ine ndikupanga za Mulungu
Mulungu akupanga zaine kukonderedwa kokhakokha
Ndikonda mmene amandikondera
Nyengo zanga amazipangira handle
Nkhondo zanga amazimenyeraa chipambano chokhachoka

Verse 1

Kuchoka tsiku lomwe ndinadziwa
Kuti mwini nkhondo alipo
Sindimadandaula
Ndidziwa chipambano chilipo
Andimenyera nkhondo mmalo mwanga ine ndili chetee zosamvetsetseka
Mpaka adani chete chete
Ndimakhala ndili pa easy
Nthawi yodandaula ndilibe
Ndimangomva zothaitha kuti adani anga agonja

Back to chorus

Melody

Verse 2

Monga momwe achitila mwana, okonderedwa ndi bambo ake
Akamenyedwa ndi azinzake, amakanenana kwa bambo akewo
Inenso chimodzimodzi, ndilibe nthawi yolimbana nanu
Olimbana nane alimbana ndabambo angawo
Olimbana nane alimbana naye
Ondikumbira dzenje adzagwera ekha
Oboola mpanda njoka idzamuluma ekha

Back to chorus

Melody

Back to chorus till end

Follow Us

More Songs From Bertha nkhoma

malawigospelmusic.com is a Christian music website with all Malawian gospel Music and any gospel News.malawigospelmusic.com offer services like song lyrics,Audio upload,poems,Music video upload on our You Tube channel called Malawian Gospel Music, Artist biography, Extended playlist (EP),Article, Album and Banner on website. For inquiry contact these numbers 0888 069 117/0885 572 836 or 0983 592 032/0994 56 15 46 or info@malawigospelmusic.com

All Rights Reserved – Designed and Developed by Kay Dee Media