Ernest Therere anabadwa pa 27 May, 1997 ndipo m’banja mwawo anabadwa ana 6 anyamata 5 wamkazi m’modzi ndipo iye ndi oyamba kubadwa.
Ernest amakhala ku Chilomoni Kwanthukwa mumzinda wa Blantyre ndipo anayamba kuyimba mu chaka cha 2018.
“Ine kuyimba ndinayamba mu chaka cha 2014 ndimayimba mu choir ya Likhubula CCAP Sunday School koma nditazindikilitsidwa kuti ndingathe kuyimba ndipomwe ndinayamba kuyimba pandekha mu chaka cha 2018” adatero Enerst.
Zimbale zomwe Enerst watulutsako ndi ziwili yoyamba mutu wake Bwezi Langa ndi Yesu ndipo yachiwili ndi Lingalila za Yesu.