Albow Banda yemwe amadziwika bwino ndi dzina lakuti Albow B pamayimbidwe anabadwa mu chaka cha 1988 ndipo m’banja mwawo anabadwa ana anayi ndipo iye ndi oyamba kubadwa.
![](https://www.malawigospelmusic.com/wp-content/uploads/2024/04/IMG-20240418-WA0004-576x1024.jpg)
Albow anayamba kuyimba m’chaka cha 2011 ndipo kufikira pano ali ndi zimbale zitatu monga Ndi Yesu Ameneyi, Mwamanga Pachani? komanso Ayoba ndipo pakatipa watulutsa nyimbo zina zatsopano zomwe zilipo 6 ndipo mayina a nyimbozo ndi monga Ndaimika Kaye, Come and see, Jerusalem iwe, Azakupeza uli pamwamba , Achulukilenji? komanso Dance and Joy.
AIbow amachokela ku Nguludi m’mudzi mwa Mataka T,A Likoswe m’boma la Chiladzulo ndipo pakadali pano akukhalira m’dziko la South Africa.