Montfort Jenala yemwe pamayimbidwe amadziwika ndi dzina lakuti MJ Monty anabadwa pa 12 April, 1985 ndipo m’banja mwawo anabadwa ana asanu ndipo iye ndi wachinayi kubadwa ndipo amakhala ku area 47 mumzinda wa Lilongwe.
![](https://www.malawigospelmusic.com/wp-content/uploads/2024/04/IMG_20240413_062104.jpg)
“Montfort anayamba kuyimba mu chaka cha 2008, “Ndimapeka nyimbo koma danga la studio m’nalibe kamba ka mapezedwe a ndalama koma patapita zaka m’nayamba kupezako ndalama kenako ndinakumana ndi Albert Khoza amenenso ndi oyimba komanso producer amene ndinamuyimbila akapela nyimbo ziwili mwa nyimbo zanga mpamene amati tiye ndikujambule chimbale ndipo kuyimba kunayambila pompo” Adatero Montfort.
Pakadali pano Montfort watulutsako zimbale zinayi ndipo mitu ya zimbalezi ndi monga Tikondane, Kachi Malawi, I believe komanso I’m Blessed chomwe ndi chimbale chatsopano chomwe chituluke ndikukhazikitsidwa mu mwezi wa June chaka chino.
![](https://www.malawigospelmusic.com/wp-content/uploads/2024/04/IMG_20240331_203227-768x1024.jpg)
Kupatula kuyimba Montfort ndi wa business komanso ali ndi company ndipo ndi Managing Director wa Nana’s Investment komanso L&L Cleaning & Landscaping services.