Saini Misoya anabadwa m’mudzi wa Sole, kuchididi boma la Nsanje.Saini Misoya anabadwa pa 14 February 1982,ndipo iyeyu anabadwa mubanja la ana khumi(10)ndipo ndimwana oyamba kubadwa.
Saini Misoya anayamba kuimba ali wachichepere maka mumakwaya ndipo mu chaka cha 2022 ndipomwe anayamba kujambula nyimbo zake zomwe pano zikumveka m’ma wailesi ena aku malawi.
Saini Misoya amakonda kwambiri zamaimbidwe chifukwa chachidwi chakechi mu 2021 anapangitsapo mpikisano wamaimbidwe omwe umadziwika kuti Misoya records gospel music competition,ndipo mu mpikisano umenewu munalowa makwaya okwana 20 ndipo number 1,2 ndi 3 ndi omwe analandira mphoto monga Keyboard ndi ndalama.Cholinga champikisanowu chinali kukweza ndikufunanso kuti uthenga wa Mulungu ufike patali kudzela m’maimbidwe.