Mike Wawoh Alibewawoh anabadwa pa 14 May 1986 ndipo m’banja mwawo mwana ndiyekha.
Mike anayamba kuyimba mu chaka cha 2000 ndipo adatulutsapo chimbale chake choyamba mu 2007 ndipo anadzayikhazikitsa ku Sheaffer mu mzinda wa Lilongwe.
Pakadali pano Mike ali mkati mojambula chimbale chake chatsopano chotchedwa Aliko Amamva chomwe akugwilira ntchito limodzi ndi Allan Chirwa,Barbra Nyangulu komanso Indonga.
Kupatula kuyimba Mike amagwira ntchito ngati Distribution komanso Logistics Manager ndi CKB Investments komanso amapanga business ndipo amakhala mu mzinda wa Blantyre.