Elisha Mbendera ndilo dzina lake lapa msonkho.Anabadwa mu chaka cha 1987 ndipo amakondwerera tsiku lakubadwa kwake pa 6 september.
Anabadwa m’banja la Bambo ndi Mayi Mbendera pomwe anabereka ana okwana 8 ndipo iye ndi wachitatu kubadwa.
Kumudzi kwawo ndi ku Ntcheu T/A Mpando, village headman Songayi koma pano wakulira akukhala ku Lilongwe.Ndi mkhristu ndipo amapemphera ku Zambezi Evangelical Church.
Kuyimba anayamba mkale kuchokera ku choir ndipo anachitika chisomo kukhalanso m’modzi wa m’nyamata odziwa kupanga backing oyimba ochuluka maka a Gospel kuno ku Malawi komanso ma international artists omwe amakhala kuti abwera mu dziko muno.
Watulutsa chimbale chimodzi chomwe chikutchedwa KULI YAHWE chomwe chikunyamula ma hit like LAKOMA BWANJI TCHIMOLO, MUKUCHITA KUMWETULIRA (Chikumbu Mtima), Wadzuka, Dziko laweruza Maso ndi Maso, Uzimu umachoka, Mundigwire dzanja, Ndimasulidwe ft Evance Mereka, Adonai komanso Ndaona.Ndi okwatira ali ndi mwana m’modzi wamamuna dzina lake Maziko Elishen Mbendera.