Cephas Kachingwe amachokela kwa T/A Ganya m’mudzi mwa chimowa m’boma la Ntcheu ndipo anabadwa pa 05-12-1983, iye ndi mwana wa chiwiri m’banja lomwe munabadwaso ana awiri.Pakadali pano amakhala ku Lilongwe kuchokela m’chaka cha 1992.
Cephas Kachingwe anayamba kuyimba m’chaka Cha 1998 pamene amayimba nawo choir yontchedwa Chisomo, kuchokela m’chaka cha 2000 Cephas anayamba kupeka nyimbo zomwe choir yi imayimba kufikila lero lino.Kupatula pa khani ya mayimbidwe Cephas Kachingwe amagwila ntchito ya zomangamanga ndipo ali ndi m’kazi m’modzi komanso ana atatu amuna awiri Misheck ndi Miracle ndi wamkazi Tabitha.