Blessed Nellie Mwale ndi M’busa wa Malawi Assemblies of God ndipo anabadwira ku Nkhotakota koma anakulira ku Lilongwe.Anabadwa pa 8/11/1987, m’banja mwawo anabadwa ana 5 ,Iyeyo ndi wa number 2 pobadwa ndipo Pastor Nellie Mwale Sali pabanja pakadali pano.
Maitanidwe a maimbidwe anamufikira ali mwana.Abambo ake amkaimba voice komanso guitar ndipo sunday lililonse amakaimba ku tsogolo ku church ndipo akakhala kunyumba abambo ake madzulo alionse amaimba ndi ana awo kuphatikizapo Nellie ndipo abambowo amapeka okha nyimbo komanso kuimba.Nellie anayamba kupeka nyimbo ali ndi zaka 15 ndipo mu 2009 anatulutsa album yotchedwa Ndamdziwa Yesu.