Praise Nkwezalamba anabadwa pa 21 November, 1985 ndipo m’banja mwawo anabadwa ana 7, iye ndi wachitatu kubadwa ndipo amachokela m’mudzi mwa Nkoma pafupi ndi ku green corner mumzinda wa Blantyre.
![](https://www.malawigospelmusic.com/wp-content/uploads/2024/04/IMG-20240419-WA0005-682x1024.jpg)
Kuyimba anayamba mkale pamene anali ndi zaka 15 koma kuyimba payekha anayamba mu chaka cha 2019 ndipo ali ndi chimbale chimodzi chotchedwa Moyo Wanga Usakaiwale chomwe anachikhazikitsa pa 5 June 2022 ku Johannesburg, m’dziko la South Africa.Praise amachokera ku Chilobwe ku Blantyre koma pakadali pano akukhalira m’dziko la South Africa.