John Masiye Ndaferankhande yemwe amadziwika ndi dzina loti John Fire pamayimbidwe anabadwa mu chaka cha 1987 ndipo m’banja mwawo anabadwa ana asanu ndipo iye ndi omaliza kubadwa.
![](https://www.malawigospelmusic.com/wp-content/uploads/2024/04/IMG-20240416-WA0035-683x1024.jpg)
John anayamba kuyimba mu chaka cha 2002 ndipo watulutsako zimbale zitatu monga Wondilenga,Emmanuelle komanso Nkumano ndipo nyimbo yatsopano yomwe wayimbira limodzi ndi Frank Chimpanzi idatuluka pa 29 March chaka chomwechino.Kupatula kuyimba John amagwira ntchito ngati Pharmacist ndipo amakhala mumzinda wa Blantyre.